2 anagulitsa cao, napatula pa mtengo wace, mkazi yemwe anadziwa, natenga cotsala, naciika pa mapazi a atumwi.
3 Koma Petro anati, Hananiya, Satana anadzaza mtima wako cifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wace wa mundawo?
4 Pamene unali nao, sunali wako kodi? ndipo pamene unaugulitsa sunali m'manja mwako kodi? bwanji cinalowa ici mumtima mwako? sunanyenga anthu, komatu Mulungu.
5 Koma Hananiya pakumva mau awa anagwa pansi namwalira: ndipo mantha akuru anagwera onse akumvawo.
6 Ndipo ananyamuka anyamata, namkulunga, namnyamula, naturuka naye, namuika.
7 Koma atapita monga maora atatu, ndipo mkazi wace, wosadziwa cidacitikaco, analowa.
8 Ndipo Petro ananena naye, Undiuze, ngati munagulitsa mundawo pa mtengo wakuti. Ndipo ananena, Inde, wakuti.