Mateyu 20 BL92

Fanizo la anchito olembedwa mwina mwina

1 Pakuti Ufumu wa Kumwamba ufanana ndi munthu mwini banja, amene anaturuka mamawa kuka lembera anchito a m'munda wace wampesa.

2 Ndipo parnene adapangana ndi anchito, pa rupiya latheka limodzi tsiku limodzi, anawatumiza ku munda wace.

3 Ndipo anaturuka dzuwa litakwera, naona ena ataima cabe pabwalo;

4 ndipo kwa iwo anati, Pitani inunso kumunda, ndipo ndidzakupatsani cimene ciri coyenera. Ndipo iwo anapita.

5 Ndiponso anaturuka usana, ndimonso popendeka dzuwa, nacita cimodzimodzi.

6 Ndipo poyandikira madzulo anaturuka, napeza ena ataima; nanena kwa iwo, Mwaimiranji kuno dzuwa lonse cabe?

7 Iwo ananena kwa iye, Cifukwa palibe munthu anatilemba. Iye anati kwa iwo, Pitani inunso ku mundawo wampesa.

8 Ndipo pamadzulo, mwini munda anati kwa kapitao wace, Kaitane anchito, nuwapatse iwo kulipira kwao, uyambe kwa omarizira kufikira kwa oyamba.

9 Ndipo pamene iwo olembedwa poyandikira madzulo anadza, analandira munthu ali yense rupiya latheka limodzi.

10 Ndipo m'mene oyamba anadza, analingalira kuti adzalandira kopambana, ndipo iwonso analandira onse rupiya latheka.

11 Koma m'mene iwo analilandira, anaderera kwa mwini banja,

12 nati, Omarizira awa anagwira nchito mphindi yaing'ono, ndipo munawalinganiza ndi ife amene tinapirira kuwawa kwa dzuwa ndi: kutentha kwace.

13 Koma iye anayankha, nati kwa mmodzi wa iwo, Mnzanga, sindikunyenga iwe; kodi iwe sunapangana ndi ine pa rupiya latheka limodzi?

14 Tenga lako, numuke; pakuti ine ndifuna kupatsa kwa uyu womarizira monga kwa iwe.

15 Sikuloleka kwa ine kodi kucita cimene ndifuna ndi zanga? Kapena diso lako laipa kodi cifukwa ine ndiri wabwino?

16 Comweco omarizira adzakhala oyamba, ndipo oyamba adzakhala omarizira.

Funso la ana a Zebedayo

17 Ndipo pamene Yesu analikukwera ku Yerusalemu, anatenga ophunzira khurni ndi awiri napita nao pa okha, ndipo panjira anati kwa iwo,

18 Onani, tikwera ku Yerusalemu; ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kwa ansembe akuru ndi alembi, ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa,

19 nadzampereka kwa anthu akunja kuti amnyoze ndi kumkwapula, ndi kumpacika; ndipo Iye adzaukitsidwa tsiku lacitatu.

20 Pomwepo anadza kwa Iye amace a ana a Zebedayo ndi ana ace omwe, namgwadira, ndi kumpempha kanthu.

21 Ndipo Iye anati kwa iye, Ufuna ciani? Iye ananena, Lamulirani kuti ana anga awiri amenewa adzakhale, wina ku dzanja lanu lao manja, ndi wina kulamanzere, mu ufumu wanu.

22 Koma Yesu anayankha nati, Inu simudziwa cimene mupempha, Kodi mukhoza kumwera cikho nditi ndidzamwere Ine? Iwo ananena kwa Iye, Ife tikhoza.

23 Iye ananena kwa iwo, Cikho canga mudzamweradi; koma kukhala ku dzanja lamanja kwangandi kulamanzere, sikuli kwanga kupatsa, koma kuli kwa iwo omwe kwakonzedweratu ndi Atate wanga.

24 Ndipo m'mene khurniwo anamva, anapsa mtima ndi abale awiriwo.

25 Koma Yesu anawaitana, nati, Mudziwa kuti mafumu a anthu amadziyesa okha ambuye ao, ndipo akuru ao amacita ufumu pa iwo.

26 Sikudzakhala comweco kwa inu ai; koma amene ali yense akafuna kukhala warnkuru mwa inu, adzakhala mtumiki wanu;

27 ndipo amene ali yense akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu:

28 monga Mwana wa munthu sanadza kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka moyo wace dipo la anthu ambiri.

Akhungu a ku Yeriko

29 Ndipo pamene iwo analikuturuka m'Yeriko, khamu lalikuru la anthu linamtsata Iye.

30 Ndipo onani, anthu akhungu awiri anakhala m'rnphepete mwa njira; m'mene iwo anamva kuti Yesu analikupitirirapo, anapfuula nati, Muticitire ife cifundo, Inu Mwana wa Davide.

31 Ndipo khamulo linawaletsa, kuti atonthole: koma anakuwitsa, nanena, Ambuye, muticitire cifundo, Inu Mwana wa Davide.

32 Ndipo Yesu anaima, nawaitana, nati, Mufuna kuti ndikucitireni ciani?

33 Ananena kwa Iye, Ambuye, kuti maso athu apenye,

34 Ndipo Yesu anagwidwa ndi cifundo, nakhudza maso ao; ndipo pornwepo anapenyanso, namtsata Iye.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28