Mateyu 9 BL92

Munthu wamanfenje wa ku Kapernao

1 Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumudzi kwao.

2 Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pachika: ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, macimo ako akhululukidwa.

3 Ndipo onani, ena a alembi ananena mumtima mwao, Uyu acitira Mulungu mwano.

4 Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Cifukwa canji mulinkuganizira zoipam'mitimayanu?

5 pakuti capafupi nciti, kunena, Macimo ako akhululukidwa; kapena kunena, Tanyamuka nuyende?

6 Koma kuti mudziwe kuti ali nazo mphamvu Mwana wa munthu pansi pano za kukhululukira macimo (pomwepo ananena kwa wodwalayo), Tanyamuka, nutenge chika lako, numuke kunyumba kwako.

7 Ndipo ananyamuka, napita ku nyumba kwace.

8 Ndipo m'mene anthu a makamu anaciona, anaopa, nalemekeza Mulungu, wakupatsa anthu mphamvu yotere.

Yesu aitana Mateyu

9 Ndipo Yesu popita, kucokera kumeneko, anaona munthu, dzina lace Mateyu, alinkukhala polandirira msonkho, nanena kwa iye, Nditsate Ine. Ndipo iye anauka, namtsata.

10 Ndipo panali pamene Iye analinkukhala pacakudya m'nyumba, onani, amisonkho ndi ocimwa ambiri anadza nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ace.

11 Ndipo Afarisi, pakuona ici, ananena kwa ophunzira ace, Cifukwa ninji Mphunzitsi wanu alinkudya pamodzi ndi amisonkho ndi ocimwa?

12 Ndipo m'mene Yesu anamva anati, Olimba safuna sing'anga ai, koma odwala.

13 Koma mukani muphunzire nciani ici:Ndifuna cifundo, si nsembe ai; pakuti sindinadza kudzaitana olungama, koma ocimwa.

Kudzikana kudya

14 Pomwepo anadza kwa Iye ophunzira ace a Yohane, nati, Cifukwa ninji ife ndi Afarisi tisala kudya kawiri kawiri, koma ophunzira anu sasala?

15 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Nanga anyamata a nyumba ya ukwati angathe kulira kodi nthawi imene mkwati akhala nao? koma adzafika masiku, pamene mkwati adzacotsedwa kwa iwo, ndipo pomwepo adzasala kudya.

16 Ndipo kulibe munthu aphathika cigamba ca nsaru yaiwisi pa copfunda cakale; pakuti cigamba cace cizomoka ku copfundaco, ndipo cicita ciboo cacikuru.

17 Kapena samathira vinyo watsopano m'matumba akale; akatero, matumba aphulika, ndi vinyo atayika, ndi matumba aonongeka: koma athira vinyo watsopano m'matumba atsopano, ndi zonse ziwiri zisungika.

Mwana wamkaziwa Yairo Mkazi wokhudza copfunda ca Yesu

18 M'mene Iye analikulankhula nao zinthu zimenezo, onani, anadza munthu mkuru, namgwadira Iye, nanena, Wamwalira tsopanolimwana wanga wamkazi, komatu mudze muike dzanja lanu pa iye, ndipo adzakhala ndi moyo.

19 Ndipo Yesu ananyamuka namtsata iye, ndi ophunzira ace omwe.

20 Ndipo onani, mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, anadza pambuyo pace, nakhudza mphonje ya copfundacace;

21 pakuti analikunena mwa iye yekha, Ngati ndingakhudze copfunda cace cokha ndidzacira.

22 Koma Yesu potembenuka ndi kuona iye anati, Limba mtima, mwana wamkaziwe, cikhulupiriro cako cakuciritsa. Ndipo mkaziyo anacira kuyambira nthawi yomweyo.

23 Ndipo Yesu polowa m'nyumba yace ya mkuruyo, ndi poona oyimba zitoliro ndi khamu la anthu obuma,

24 ananena, Turukani, pakuti kabuthuko sikanafa koma kali m'tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.

25 Koma pamene khamulo linaturutsidwa, Iye analowamo, nagwira dzanja lace; ndipo kabuthuko kadauka.

26 Ndipo mbiri yace imene inabuka m'dziko lonse limenelo.

Yesu aciritsa akhungu awiri ndi wosalankhula

27 Ndipo popita Yesu kucokera kumeneko, anamtsata Iye anthu awiri akhungu, opfuula ndi kuti, Muticitire ife cifundo, mwana wa Davide.

28 Ndipo m'mene Iye analowa m'nyumbamo, akhunguwo anadza kwa Iye; ndipo Yesu anati kwa iwo, Mukhulupirira kodi kuti ndikhoza kucita ici? Anena kwa Iye, Inde, Ambuye.

29 Pomwepo anakhudza maso ao, nati, Cicitidwe kwa inu monga cikhulupiriro canu.

30 Ndipo maso ao anaphenyuka. Ndipo Yesu anawauzitsa Iwo, nanena, Yang'anirani, asadziwe munthu ali yense.

31 Koma iwo anaturukamo, nabukitsa mbiri yace m'dziko lonselo.

32 Ndipo pamene iwo analikuturuka, onani, anabwera naye kwa Iye munthu wosalankhula, wogwidwa ndi ciwanda.

33 Ndipo m'mene cinaturutsidwa ciwandaco, wosalankhulayo analankhula, ndipo makamu a anthu anazizwa, nanena, Kale lonse sicinaoneke comweco mwa Israyeli.

34 Koma Afarisi analinkunena, Aturutsa ziwanda ndi mphamvu zace za mfumu ya ziwanda.

Zotuta ndi anchito

35 Ndipo Yesu anayendayenda m'mizinda yonse ndi m'midzi, namaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalalikira uthenga wabwino wa Ufumuwo, naciritsa nthenda iri yonse ndi zofoka zonse.

36 Koma Iye, poona makamuwo, anagwidwa m'mtima ndi cisoni cifukwa ca iwo, popeza anali okambululudwa ndi omwazikana, akunga nkhosa zopanda mbusa.

37 Pomwepo ananena kwa ophunzira ace, Zotuta zicurukadi koma anchito ali owerengeka.

38 Cifukwa cace pempherani Mwini zotuta kuti akokose anchito kukututakwace.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28