Mateyu 3 BL92

Yohane Mbatizi

1 Ndipo masiku aja anadza Yohane Mbatizi, nalalikira m'cipululu ca Yudeya,

2 nanena, Tembenukani mitima; cifukwa Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

3 Pakuti uyu ndiye ananenayo Yesaya mneneri, kuti,Mau a wopfuula m'cipululu,Konzani khwalala la Ambuye,Lungamitsani njira zace.

4 Ndipo Yohane yekhayo anali naco cobvala cace ca ubweya wangamila, ndi lamba lacikopa m'cuuno mwace; ndi cakudya cace cinali dzombe ndi uci wa kuthengo.

5 Pamenepo panamturukira iye ku Yerusalemu, ndi Yudeya lonse, ndi dziko lonse loyandikana ndi Yordano;

6 nabatizidwa ndi iye mu mtsinjewo wa Yordano, alikuulula macimo ao.

7 Ndipo iye pakuona ambiri a Afarisi ndi a Asaduki akudza ku ubatizo wace, anati kwa iwo, Obadwa a njoka inu, ndani anakulangizani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8 Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:

9 ndipo musamayesa kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye Abrahamu; pakuti ndinena kwa inu kuti mwa miyala iyi Mulungu akhoza kuukitsira Abrahamu ana.

10 Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cifukwa cace mtengo uli wonse wosabala zipatso zabwino udulidwa nuponyedwa pamoto,

11 Inetu ndikubatizani inu ndi madzi kuloza ku kutembenuka mtima; koma Iye wakudza pambuyo panga, ali wakundiposa mphamvu, amene sindiyenera kunyamula nsapato zace: Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto:

12 couluzira cace ciri m'dzanja lace, ndipo adzayeretsa padwale pace; ndipo adzasonkhanitsa tirigu wace m'ciruli, koma mankhusu adzatentha ndi moto wosazima.

Abatizidwa Yesu

13 Pamenepo Yesu anacokera ku Galileya nadza ku Yordano kwa Yohane, kudzabatizidwa ndi iye.

14 Koma Yohane anati amkanize, nanena, Ndiyenera ine kubatizidwa ndi Inu, ndipo Inu mudza kwa ine kodi?

15 Koma Yesu anayankha, nati kwa iye, Balola tsopano: pakuti kuyenera ife kukwaniritsa cilungamo conse motero. Pamenepo anamlola Iye.

16 Ndipo Yesu, pamene anabatizidwa, pomwepo anaturuka m'madzi: ndipo onani, miyamba inamtsegukira Iye, ndipo anapenya Mzimu wa Mulungu wakutsika ngati nkhunda nudza nutera pa Iye;

17 ndipo onani, mau akucokera kumiyamba akuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa Iyeyu ndikondwera.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28