11 wacisanu ndi cimodzi Atai, wacisanu ndi ciwiri Elieli,
12 wacisanu ndi citatu Yohanani, wacisanu ndi cinai Elzabadi,
13 wakhumi Yeremiya, wakhumi ndi cimodzi Makibanai.
14 Awa a ana a Gadi, anali atsogoleri a nkhondo; wamng'ono wa iwo anayang'anira zana limodzi, ndi wamkuru wa iwo anayang'anira cikwi cimodzi.
15 Awa ndi omwe aja anaoloka Yordano mwezi woyamba, atadzala kusefukira magombe ace onse; nathawitsa onse okhala m'zigwa kum'mawa ndi kumadzulo.
16 Ndipo anadza ena a ana a Benjamini ndi Yuda kulinga kwa Davide.
17 Ndipo Davide anaturuka kukomana nao, nayankha, nanena nao, Ngati mwandidzera mwamtendere kundithandiza, mtima wanga udzalumikizana nanu; koma ngati mwafika kundipereka kwa adani anga, popeza m'manja mwanga mulibe ciwawa, Mulungu wa makolo athu acione ndi kucilanga.