1 Ndipo Hiramu mfumu ya Turo anatumiza mithenga kwa Davide, ndi mikungudza, ndi amisiri omanga miyala, ndi amatabwa, kuti ammangire nyumba.
2 Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova adamkhazikitsa mfumu ya Israyeli; pakuti ufumu wace unakwezekadi, cifukwa ca anthu ace Israyeli.
3 Ndipo Davide anatenga akazi ena ku Yerusalemu, nabala Davide ana amuna ndi akazi ena.
4 Maina a ana anali nao m'Yerusalemu ndi awa: Samna, ndi Sobabu Natani, ndi Solomo,
5 ndi Ibara, ndi Elisua, ndi Elipeleti,