3 Ndipo Davide anatenga akazi ena ku Yerusalemu, nabala Davide ana amuna ndi akazi ena.
4 Maina a ana anali nao m'Yerusalemu ndi awa: Samna, ndi Sobabu Natani, ndi Solomo,
5 ndi Ibara, ndi Elisua, ndi Elipeleti,
6 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,
7 ndi Elisama, ndi Beliyada, ndi Elifeleti.
8 Pamene Afilisti anamva kuti anamdzoza Davide akhale mfumu ya Aisrayeli onse, Afilisti onse anakwera kufunafuna Davide; ndipo Davide anamva, nawaturukira.
9 Afilisti tsono anafika, nafalikira m'cigwa ca Refaimu.