29 Mcitireni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani pamaso pace;Lambirani Yehova m'ciyero cokometsetsa,
30 Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi,Dziko lokhalamo anthu lomwe lakhazikika, kuti silingagwedezeke.
31 Kukondwerere kumwamba, ndi dziko lapansi lisekerere;Anene mwa amitundu, Yehova acita ufumu.
32 Nyanja ikukume m'kudzala kwace,Munda ukondwerere, ndi zonse ziri m'mwemo;
33 Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera pamaso pa Yehova;Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi,
34 Yamikani Yehova; pakuti iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.
35 Nimunene, Tipulumutseni, Mulungu wa cipulumutso cathu;Mutisokolotse ndi kutilanditsa kwa amitundu,Kuti tiyamike dzina lanu loyera,Ndi kudzitamandira naco cilemekezo canu.