3 Ndipo Davide anakantha Hadarezeri mfumu ya Zoba ku Hamati, pomuka iye kukhazikitsa ulamuliro wace ku mtsinje wa Firate.
4 Ndipo Davide analanda magareta ace cikwi cimodzi, ndi apakavalo zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi awiri; Davide anadula mitsita akavalo onse okoka magareta, koma anasungako ofikira magareta zana limodzi.
5 Ndipo Aaramu a ku Damasiko anadza kudzathandiza Hadarezeri mfumu ya Zoba; koma Davide anakantha Aaramu amuna zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.
6 Ndipo Davide anaika asilikari a boma m'Aramu wa Damasiko; ndi Aaramu anasanduka anthu a Davide, nabwera nazo mphatso, Ndipo Yehova anasunga Davide kuli konse anamukako.
7 Natenga Davide zikopa zagolidi zinali pa anyamata a Hadarezeri, nabwera nazo ku Yerusalemu.
8 Ndi ku Tibati, ndi ku Kuni, midzi ya Hadarezeri, Davide anatenga mkuwa wambiri, ndiwo umene Solomo anayenga nao thawale lamkuwa, ndi nsanamira, ndi zipangizo zamkuwa.
9 Ndipo pakumva Tou, mfumu ya ku Hamati, kuti Davide adakantha khamu lonse la Hadarezeri mfumu ya ku Zoba,