27 Ndipo Yehova anauza wamthenga kuti abweze lupanga lace m'cimace.
28 Nthawi yomweyi, pakuona Davide kuti Yehova anambvomereza pa dwale la Orinani Myebusi, anaphera nsembe pomwepo.
29 Pakuti kacisi wa Yehova amene Mose anapanga m'cipululu, ndi guwa la nsembe yopsereza, zinali pa msanje wa ku Gibeoni nthawi yomweyi.
30 Kama Davide sanathe kumuka kukhomo kwace kufunsira kwa Mulungu, pakuti anaopa lupanga la mthenga wa Yehova.