24 Awa ndi ana a Levi monga mwa nyumba za makolo ao, ndiwo akuru a nyumba za makolo a iwo owerengedwa mwa ciwerengo ca maina mmodzi mmodzi, akugwira nchito ya utumiki wa nyumba ya Yehova, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.
25 Pakuti Davide anati, Yehova Mulungu wa Israyeli wapumulitsa anthu ace; ndipo akhala m'Yerusalemu kosatha;
26 ndiponso Alevi asasenzenso kacisi ndi zipangizo zace zonse za utumiki wace.
27 Pakuti monga mwa mau ace otsiriza a Davide, ana a Levi anawerengedwa kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.
28 Pakuti nchito yao ndiyo kuimirira ana a Aroni, atumikire m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo, ndi kuzipinda, ndi kuyeretsa zopatulika zonse; inde nchito za utumiki wa nyumba ya Mulungu;
29 ya mkate woonekera womwe, ndi ya ufa wosalala wa nsembe yaufa, ndi ya timitanda taphanthiphanthi topanda cotupitsa, ndi ya ciwaya, ndi yakukazinga, ndi ya miyeso iri yonse;
30 ndi kuimirira m'mawa ndi m'mawa kuyamika ndi kulemekeza Yehova, momwemonso madzulo;