7 A Agerisomu: Ladani ndi Simeyi,
8 Ana a Ladani: wamkuru ndi Yehieli, ndi Zethamu, ndi Yoeli; atatu.
9 Ana a Simeyi: Selomoti, ndi Hazieli, ndi Hanani; atatu. Ndiwo akuru a nyumba za makolo a Ladani.
10 Ndi ana a Simeyi: Yahati, Zina, ndi Yeusi, ndi Beriya. Awa anai ndiwo ana a Simeyi.
11 Wamkuru wa iwo ndi Yahati, mnzace ndi Ziza; koma Yeusi ndi Beriya analibe ana ambiri, potero anakhala nyumba ya kholo yowerengedwa pamodzi.
12 Ana a Kohati: Amiramu, Izara, Hebroni, ndi Uzieli; anai.
13 Ana a Amiramu: Aroni, ndi Mose; ndipo Aroni anasankhidwa kuti apatule zopatulikitsa, iye ndi ana ace, kosalekeza, kufukiza pamaso pa Yehova, kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kosatha.