1 A magawidwe a odikira a Akora: Meselemiya mwana wa Kore wa ana a Asafu.
2 Ndipo Meselemiya anali ndi ana, woyamba Zekariya, waciwiri Yedyaeli, wacitatu Zebadiya, wacinai Yatiniyeli,
3 wacisanu Elamu, wacisanu ndi cimodzi Yohanana, wacisanu ndi ciwiri Elihunai.
4 Ndipo Obedi Edomu anali nao ana, woyamba Semaya, waciwiri Yozabadi, wacitatu Yowa, wacinai Sakara, wacisanu Netaneli,
5 wacisanu ndi cimodzi Amiyeli, wacisanu ndi ciwiri Isakara, wacisanu ndi citatu Peuletai; pakuti Mulungu adamdalitsa.
6 Kwa Semaya mwana wace yemwe kunabadwa ana, akulamulira nyumba ya atate wao; pakuti anali ngwazi zamphamvu.