14 Wakhumi ndi cimodzi wa mwezi wakhumi ndi cimodzi ndiye Benaya Mpiratoni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
15 Wakhumi ndi ciwiri wa mwezi wakhumi ndi ciwiri ndiye Heledai Mnetofati wa Otiniyeli; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
16 Koma oyang'anira mafuko a lsrayeli ndi awa: wa Arubeni mtsogoleri wao ndiye Eliezeri mwana wa Zikiri; wa Asimeoni, Sefatiya mwana wa Maaka;
17 wa Alevi, Hasabiya mwana wa Kemueli; wa Aroni, Zadoki;
18 wa Yuda, Elihu mbale wina wa Davide; wa Isakara, Omri mwana wa Mikaeli;
19 wa Zebuluni, Isimaya mwana wa Obadiya; wa Nafitali, Yeremoti mwana wa Azrieli;
20 wa ana a Efraimu, Hoseya mwana wa Azaziya; wa pfuko la Manase logawika pakati, Yoeli mwana wa Pedaya;