7 Wacinai wa mwezi wacinai ndiye Asebeli mbale wa Yoabu, ndi pambuyo pace Zebadiya mwana wace; ndi m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.
8 Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
9 Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
10 Wacisanu ndi ciwiri wa mwezi wacisanu ndi ciwiri ndiye Helezi Mpeloni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
11 Wacisanu ndi citatu wa mwezi wacisanu ndi citatu ndiye Sibekai Mhusati wa Afera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
12 Wacisanu ndi cinai wa mwezi wacisanu ndi cinai ndiye Abiezeri M-anatoti wa Abenjamini; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
13 Wakhumi wa mwezi wakhumi ndiye Maharai Mnetofati wa Azera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.