40 Ndipo anapeza podyetsa ponenepetsa ndi pabwino, ndipo dzikoli ndi lacitando ndi lndikha ndi losungikamo, pakuti okhalako kale ndiwo a Hamu.
41 Iwo tsono olembedwa maina anadza masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda, nakantha mahema ao ndi zokhalamo zao, naziononga konse mpaka lero, nakhala m'malo mwao; popeza panali podyetsa zoweta zao pamenepo.
42 Ndipo ena a iwowa a ana a Simeoni, amuna mazana asanu, anamka ku phiri la Seiri; akuwatsogolera ndiwo Pelatiya, ndi Neariya, ndi Refaya, ndi Uzieli; ana a lsi.
43 Nakantha otsala a Aamaleki adapulumukawo, nakhala komweko mpaka lero lino.