15 ndi Makiri anadzitengera mkazi, mlongo wace wa Hupimu ndi Supimu, dzina lace ndiye Maaka. Ndipo dzina la mwana waciwiri wa Manase ndiye Tselofekadi. Ndi Tselofekadi anali ndi ana akazi.
16 Ndi Maaka mkazi wa Makiri anabala mwana, namucha dzina lace Peresi, ndi dzina la mbale wace ndiye Seresi, ndi ana ace ndiwo Ulamu, ndi Rakemu.
17 Ndi mwana wa Ulamu: Bedani; ndiwo ana a Gileadi mwana wa Makiri mwana wa Manase.
18 Ndi mlongo wace Hamoleketi anabala Isodi, ndi Abiezeri, ndi Mala.
19 Ndi ana a Semida ndiwo Ahiani, ndi Sekemu, ndi Liki, ndi Aniamu.
20 Ndi ana a Efraimu: Sutera, ndi Beredi mwana wace, ndi Tahati mwana wace, ndi Ekada mwana wace, ndi Tahati mwana wace,
21 ndi Zabadi mwana wace, ndi Sutela mwana wace, ndi Ezeri, ndi Eleadi, amene anthu a Gadi obadwa m'dziko anamupha, popeza anatsikira kukalanda zoweta zao.