7 Ndipo mtengo wa mkondo wace unali ngati mtanda woombera nsaru; ndi khali la mkondowo linalemera ngati masekeli mazana asanu ndi limodzi a citsulo; ndipo womnyamulira cikopa anamtsogolera.
8 Naima iye naitana makamu a nkhondo a Israyeli, nanena nao, Munaturukiranji kundandalitsa nkhondo yanu? Sindine Mfilisti kodi, ndi inu anyamata a Sauli? mudzisankhire munthu, atsikire kwa ine.
9 Akakhoza iyeyo kuponyana ndi ine ndi kundipha, tidzakhala ife akapolo anu; koma ine ndikamlaka, ndi kumupha, tsono mudzakhala inu akapolo athu, ndi kutitumikira ife.
10 Nati Mfilistiyo, Ine ndinyoza makamu a nkhondo a Israyeli lero; mundipatse munthu, kuti tilimbane ife awiri.
11 Ndipo pamene Sauli ndi Aisrayeli onse anamva mau ao a Mfilistiyo, anadodoma, naopa kwambiri.
12 Tsono Davide anali mwana wa M-efrati uja wa ku Betelehemu-Yuda, dzina lace ndiye Jese; ameneyu anali nao ana amuna asanu ndi atatu; ndipo m'masiku a Sauli munthuyo anali nkhalamba, mwa anthu.
13 Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.