12 Yehova aweruze pakati pa ine ndi inu; ndipo Yehova adzandibwezera cilango kwa inu; koma dzanja langa silidzakhala pa inu.
13 Monga umanena mwambi wa makolo, kuti, Ucimo uturukira mwa ocimwa; koma dzanja langa silidzakhala pa inu.
14 Nanga mfumu ya Israyeli inaturukira yani; inu mulikupitikitsa yani? Garu wakufa, kapena nsabwe.
15 Cifukwa cace Yehova akhale woweruza, naweruze pakati pa ine ndi inu, nayang'anire, oandigwirire moyo, oandipulumutse m'dzanja lanu.
16 Ndipo kunali, pakutsiriza Davide kulankhula mau awa kwa Sauli, Sauli anati, Ndiwo mau ako kodi, mwana wanga Davide? Sauli nakweza mau ace, nalira misozi.
17 Nati kwa Davide, Iwe ndiwe wolungama woposa ine; popeza unandibwezera zabwino, koma ine ndinakubwezera zoipa.
18 Ndipo unatsimikiza lero lino kuti wandicitira zabwino cifukwa sunandipha pamene Yehova anandipereka m'dzanja lako.