7 Ndipo pamene Aisrayeli akukhala tsidya lina la cigwa, ndi iwo akukhala tsidya la Yordano, anaona kuti Aisrayeli alikuthawa, ndi kuti Sauli ndi ana ace anafa, iwowa anasiya midzi yao, nathawa; ndipo Afilisti anadza nakhala m'menemo.
8 Ndipo kunali m'mawa mwace, pakubwera Afilisti kubvula akufawo, anapeza Sauli ndi ana ace atatu ali akufa m'phiri la Giliboa.
9 Ndipo anadula mutu wace, natenga zida zace, natumiza m'dziko lonse la Afilisti mithenga yolalikira ku nyumba ya milungu yao, ndi kwa anthu.
10 Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya Asitarote; napacika mtembo wace ku linga la ku Betisani.
11 Koma pamene a ku Jabezi Gileadi anamva zimene Afilisti anamcitira Sauli,
12 ngwazi zonse zinanyamuka ndi kucezera usiku kuyenda, natenga mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, pa linga la Betisani; nafika ku Jabezi Gileadi naitentha kumeneko.
13 Natenga mafupa ao nawaika patsinde pa mtengo uli m'Jabezi, nasala kudya masiku asanu ndi awiri.