2 Mwenzi atayesa bwino cisoni canga,Ndi kuika matsoka anga pamodzi pamuyeso!
3 Pakuti zikadalemera tsopano koposa mcenga wa kunyanja;Cifukwa cace mau anga ndasonthokera kunena.
4 Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa,Mzimu wanga uumwa ulembe wace;Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.
5 Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?
6 Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere?Coyera ca dzira cikolera kodi?
7 Zimene moyo wanga ukana kuzikhudzaZikunga cakudya cosakolera kwa ine.
8 Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!