4 Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa,Mzimu wanga uumwa ulembe wace;Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.
5 Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?
6 Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere?Coyera ca dzira cikolera kodi?
7 Zimene moyo wanga ukana kuzikhudzaZikunga cakudya cosakolera kwa ine.
8 Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!
9 Cimkomere Mulungu kundiphwanya,Alole dzanja lace lindilikhel
10 Pamenepo ndidzasangalala,Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka;Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.