4 Ndipo khamu la mudziwo linagawikana; ena analindi Ayuda, komaena anali ndi atumwi.
5 Ndipo pamene panakhala cigumukiro ca Ahelene ndi ca Ayuda ndi akuru ao, ca kuwacitira cipongwe ndi kuwaponya miyala,
6 iwo anamva, nathawira ku midzi ya Lukaoniya, Lustra ndi Derbe, ndi dziko lozungulirapo:
7 kumeneko ndiko Uthenga Wabwino.
8 Ndipo pa Lustra panakhala munthu wina wopanda mphamvu ya m'mapazi mwace, wopunduka cibadwire, amene sanayenda nthawi zonse.
9 Ameneyo anamva Paulo alinkulankhula; ndipo Paulo pomyang'anitsa, ndi kuona kuti anali ndi cikhulupiriro colandira naco moyo,
10 anati ndi mau akuru, Taimirira. Ndipo iyeyu anazunzuka, nayenda.