12 Ndipo khamu lonse linatonthola; ndipo anamvera Bamaba ndi Paulo alikubwerezanso zizindikiro ndi zozizwitsa zimene Mulungu anacita nao pa amitundu.
13 Pamene iwo anatonthola Yakobo anayankha, nati,Abale, mverani ine:
14 Sumeoni wabwereza kuti poyamba Mulungu anayang'anira amitundu, kuti atenge mwa iwo anthu a dzina lace.
15 Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,
16 Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa;Ndidzamanganso zopasuka zace,Ndipo ndidzaciimikanso:
17 Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,
18 Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.