1 Ndipo panali, pamene Apolo anali ku Korinto, Paulo anapita pa maiko a pamtunda, nafika ku Efeso, napeza akuphunzira ena;
2 ndipo anati kwa iwo, Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupira? Ndipo anati, lai, sitinamva konsekuti Mzimu Woyera waperekedwa.
3 Ndipo anati, Nanga mwabatizidwa m'ciani? Ndipo anai, Mu ubatizo wa Yohane.
4 Ndipo anati Paulo, Yohane anabatiza ndi ubatizo wa kutembenuka mtima, nati kwa anthu, kuti amkhulupirire iye amene adzadza pambuyo pace, ndiye Yesu.
5 Pamene anamva ici, anabatizidwa m'dzina la Ambuye Yesu.
6 Ndipo pamene Paulo anaika manja ace pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.