1 Ndipo atapita masiku asanu anatsika mkulu wa ansembe Hananiya pamodzi ndi akuru ena, ndi wogwira moyo dzina lace Tertulo; ndipo anafotokozera kazembeyo za kunenera Paulo.
2 Ndipo pamene adamuitana, Tertulo anayamba kumnenera ndi kunena.Popeza tiri nao mtendere wambiri mwa inu, ndipo mwa kuganiziratu kwanu muukonzera mtundu wathu zotiipsa,
3 tizilandira ndi ciyamiko conse, monsemo ndi ponsepo, Felike womveka inu.
4 Koma kuti ndingaonjeze kukulemetsani ndikupempha, ni mutimvere mwacidule ndi cifatso canu.
5 Pakuti tapeza munthuyu ali ngati mliri, ndi woutsa mapanduko kwa Ayuda onse m'dziko lonse lokhalamo anthu, ndi mtsogoleri wa mpanduko wa Anazarene;
6 amenenso anayesa kuipsa Kacisi; amene tamgwira;