1 Ndipo pamene padatsimikizika kuti tipite m'ngalawa kunka ku Italiya, anapereka Paulo ndi andende ena kwa kenturiyo dzina lace Yuliyo, wa gulu la Augusto.
2 Ndipo m'mene tidalowam'ngalawa ya ku Adramutiyo ikati ipite kunka ku malo a ku mbali ya Asiya, dnakankha, ndipo Aristarko Mmakedoniya wa ku Tesalonika, anali nafe.
3 Ndipo m'mawa mwace tinangokoceza ku Sidoni; ndipo Yuliyo anacitira Paulo mwacikondi, namlola apite kwa abwenzi ace amcereze.
4 Ndipo pokankhanso pamenepo, tinapita kutseri kwa Kupro, popeza mphepo inaomba mokomana nafe.
5 Ndipo pamene tidapyola nyanja ya kunsi kwace kwa Kilikiya ndi Pamfiliya, tinafika ku Mura wa Lukiya.
6 Ndipo kenturiyo anapezako ngalawa ya ku Alesandriya, irikupita ku Italiya, ndipo anatilongamo.
7 Ndipo m'mene tidapita pang'ono pang'ono masiku ambiri, ndi kufika mobvutika pandunji pa Knido, ndipo popeza siinatilolanso mphepo, tinai pita m'tseri mwa Krete, pandunji pa Salimone;