1 Ndipo titapulumuka, pamenepo tinadziwa kuti cisumbuco cinachedwa Melita.
2 Ndipo akunja anaticitira zokoma zosacitika pena ponsepo; pakuti anasonkha moto, natilandira ife tonse, cifukwa ca mvula inalinkugwa, ndi cifukwa ca cisanu.
3 Koma pamene Paulo adaola cisakata ca nkhuni, naciika pamoto, inaturukamo njoka, cifukwa ca kutenthaku, nilumadzanja lace.
4 Koma pamene akunjawo anaona ciromboco ciri lende pa dzanja lace, ananena wina ndi mnzace, Zoona munthuyu ndiye wambanda, angakhale anapulumuka m'nyanja, cilungamo sicimlola akhale ndi moyo.