33 Ndipo atumwi anacita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali cisomo cacikuru pa iwo onse.
34 Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; 1 pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ace a izo adazigulitsa,
35 2 nawaika pa mapazi a atumwi; ndipo anagawira yense monga kusowakwace.
36 Ndipo Yosefe, wochedwa ndi atumwi Bamaba (ndilo losandulika mwana wa cisangalalo), Mlevi, pfuko lace la ku Kupro,
37 pokhala nao munda, anaugulitsa, nabwera nazo ndalama zace, 3 naziika pa mapazi a atumwi.