4 Koma ambiri a iwo amene adamva mau anakhulupira; ndipo ciwerengero ca amuna cinali ngati zikwi zisanu.
5 Koma panali m'mawa mwace, anasonkhana pamodzi m'Yerusalemu oweruza, ndi akulu, ndi alembi;
6 ndi Anasi mkulu wa ansembe, ndi Kayafa, ndi Yohane, ndi Alesandro, ndi onse amene anali a pfuko la mkulu waansembe.
7 Ndipo m'mene anawaimika pakati, anafunsa kuti, Ndi mphamvu yanji, kapena m'dzina lanji, mwacita ici inu?
8 Pamenepo Petro, wodzala ndi Mzimu Woyera anati kwa iwo, Oweruza a anthu inu, ndi akulu,
9 ngati ife lero tiweruzidwa cifukwa ca nchito yabwino ya pa munthu wodwala, ndi maciritsidwe ace,
10 zindikirani inu nonse, ndi anthu onse a Israyeli, kuti m'dzina la Yesu Kristu Mnazarayo, amene inu munampacika pamtanda, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa, mwa Iyeyu munthuyu aimirirapo pamaso panu, wamoyo.