37 ]
38 Ndipo anamuuza kuti aimitse gareta; ndipo anatsikira onse awiri kumadzi, Filipo ndi mdindoyo; ndipoanambatiza iye.
39 Ndipo pamene anakwera kururuka m'madzi, Mzimu wa Ambuye anakwatula Filipo; ndipo mdindo sanamuonanso, pakuti anapita njira yace wokondwera.
40 Koma Filipo anapezedwa ku Azotu; ndipo popitapitaanalalikira Uthenga Wabwino m'midzi yonse, kufikira anadza iye ku Kaisareya.