10 Hosa yemwe wa ana a Merari anali ndi ana, wamkuru ndi Simri; pakuti ngakhale sanali wobadwa woyamba, atate wace anamuyesa wamkuru;
11 waciwiri Hilikiya, wacitatu Tebaliya, wacinai Zekariya; ana ndi abale onse a Hosa ndiwo khumi ndi atatu.
12 Mwa iwowa munali magawidwe a odikira, mwa akulu a amuna akucita udikiro wao, monga abale ao, kutumikira m'nyumba ya Yehova.
13 Ndipo anacita maere ang'ono ndi akuru, monga mwa nyumba za makolo ao, kucitira zipata zonse.
14 Ndi maere a kum'mawa anagwera Selemiya. Ndipo anacitira maere Zekariya mwana wace, phungu wanzeru, ndi maere anamgwera kumpoto;
15 Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.
16 Supimu ndi Hosa kumadzulo, ku cipata ca Saleketi, ku mseu wokwerapo, udikiro pandunji pa udikiro.