10 Ndipo kunali m'mawa mwace, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu unamgwira Sauli mwamphamvu, iye nalankhula moyaruka m'nyumba yace; koma Davide anayimba ndi dzanja lace, monga amacita tsiku ndi tsiku; koma m'dzanja la Sauli munali mkondo.
11 Ndipo Sauli anaponya mkondowo; pakuti anati, Ndidzapyoza Davide ndi kumphatikiza ndi khoma. Ndipo Davide analewa kawiri kucoka pamaso pace.
12 Ndipo Sauli anaopa Davide, cifukwa Yehova anali naye, koma adamcokera Sauli.
13 Cifukwa cace Sauli anamcotsa kuti asakhale naye, namuika akhale mtsogoleri wace wa anthu cikwi cimodzi; ndipo iye anatsogolera anthu kuturuka ndi kubwera nao.
14 Ndipo Davide anakhala wocenjera m'mayendedwe ace onse; ndipo Yehova anali naye.
15 Ndipo pamene Sauli anaona kuti analikukhala wocenjera ndithu anamuopa.
16 Koma Aisrayeli onse ndi Ayuda onse anamkonda Davide pakuti anawatsogolera kuturuka ndi kulowa nao.