6 Pakumva Sauli kuti anadziwika Davide, ndi anthu ace akukhala naye, Sauti analikukhala m'Gibeya, patsinde pa mtengo wa kumsanje, m'dzanja lace munali mkondo wace, ndi anyamata ace onse anaimirira pali iye.
7 Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace akuima comzinga, Imvani tsopano, inu a Benjamini; kodi mwana wa Jese adzakupatsani inu nonse minda, ndi minda yamphesa, kodi adzakuikani mukhale atsogoleri a zikwi ndi a mazana;
8 kuti inu nonse munapangana dwembu pa ine, ndipo palibe wina wakundiululira kuti mwana wanga anapangana pangano ndi mwana wa Jese, ndipo palibe wilia wa inu wakundidtira cifundo kapena kundidziwitsa kuti mwana wanga anafulumiza mnyamata wanga kundilalira monga lero lomwe?
9 Pamenepo Doegi wa ku Edomu, anaimirira ndi anyamata a Sauli, nayankha, nati, Ine ndinamuona mwana wa Jeseyo alikufika ku Nobi, kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubu.
10 Ndipo iye anamfunsira kwa Yehova, nampatsa cakudya, nampatsanso lupanga la Gotiate Mfilistiyo.
11 Pamenepo mfumu anatuma mthenga kukaitana Ahimeleki wansembeyo, mwana wa Ahitubu, ndi banja lonse la atate wace, ansembe a ku Nobi; ndipo iwo onse anafika kwa mfumu.
12 Ndipo Sauli anati, Imva tsopano iwe mwana wa Ahitubu. Nayankha iye, Ndine, mbuye wanga.