1 Pamenepo mzimu wa Mulungu unagwera Azariya mwana wa Odedi,
2 ndipo anaturuka kukomana naye Asa, nanena naye, Mundimvere, Asa, ndi onse Ayuda ndi Abenjamini, Yehova ali nanu; mukakhala ndi Iye, mukamfuna Iye, mudzampeza; koma mukamsiya, adzakusiyani.
3 Masiku ambiri tsono Israyeli anakhala wopanda Mulungu woonayo, ndi wopanda wansembe wakuphunzitsa, ndi wopanda cilamulo;
4 koma pamene anatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli m'kusautsidwa kwao, ndi kumfuna, anampeza.