7 Ndipo ndinamvanso mau akunena ndi ine, Tauka Petro; ipha, nudye.
8 Koma ndinati, Iaitu, Ambuye; pakuti kanthu wamba, kapena konyansa sikanalowe m'kamwa mwanga ndi kale lonse.
9 Koma mau anayankha nthawi yaciwiri oturuka m'mwamba, Cimene Mulungu anaciyeretsa, usaciyesera cinthu wamba.
10 Ndipo ici cinacitika katatu; ndipo zinakwezekanso zonse kumwamba.
11 Ndipo taonani, pomwepo amuna atatu anaima pa khomo la nyumba m'mene munali ife, anatumidwa kwa ine ocokera ku Kaisareya.
12 Ndipo Mzimu anandiuza ndinke nao, wosasiyanitsa konse. Ndipo abale awa asanu ndi mmodzi anandiperekezanso anamuka nane; ndipo tinalowa m'nyumba ya munthuyo;
13 ndipo anatiuza ife kuti adaona mngelo wakuimirira m'nyumba yace, ndi kuti, Tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni, wonenedwanso Petro;