13 Ndipo m'mene anagogoda pa citseko ca pakhomo, linadza kudzabvomera buthu, dzina lace Roda.
14 Ndipo pozindikira mau ace a Petro, cifukwa ca kukondwera sanatsegula pakhomo, koma anathamanga nalowanso, nawauza kuti Petro alikuima pakhomo.
15 Koma anati kwa iye, Wamisala iwe. Ndipo analimbika ndi kunena kuti nkutero. Ndipo ananena, Ndiye mngelo wace.
16 Koma Petro anakhala cigogodere; ndipo m'mene adamtsegulira, anamuona iye, nadabwa.
17 Koma m'mene adawatambasulira dzanja akhale cete, anawafotokozera umo, adamturutsira Ambuye m'ndende. Ndipo anati, Muwauze Yakobo ndi abale izi, Ndipo anaturuka napita kwina.
18 Koma kutaca, panali phokoso lalikuru mwa asilikari, Petro wamuka kuti.
19 Ndipo pamene Herode adamfunafuna, wosampeza, anafunsitsa odikira nalamulira aphedwe. Ndipo anatsika ku Yudeya kunka ku Kaisareya, nakhalabe kumeneko.