2 Ameneyo anamcitira umboni wabwino abale a ku Lustra ndi Ikoniyo.
3 Iyeyo Paulo anafuna kuti amuke naye, ndipo anamtenga, namdula, cifukwa ca Ayuda amene anakhala m'maikomo; pakuti onse anadziwa kuti atate wace anali Mhelene.
4 Pamene anapita kupyola pamidzi, anapereka kwa iwo malamulo awasunge, amene analamulira atumwi ndi akuru a pa Yerusalemu.
5 Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku ndi tsiku.
6 Ndipo anapita pa dziko la Frugiya ndi Galatiya, atawaletsa Mzimu Woyera kuti asalalikire mau m'Asiya; pamene anafika kundunji kwa Musiya,
7 anayesa kunka ku Bituniya; ndipo Mzimu wa Yesu sanawaloleza;
8 ndipo pamene anapita pambali pa Musiya, anatsikira ku Trowa.