15 Ndipo unayankha mzimu woipa, nuti kwa iwo, Yesu ndimzindikira, ndi Paulo ndimdziwa, koma inu ndinu ayani?
16 Ndipo munthu, mwa iye amene munali mzimu woipa, anawalumphira nawaposa, nawalaka onse awiriwo, kotero kuti anathawa m'nyumba amarisece ndi olasidwa.
17 Zimenezo zidamveka kwa onse, Ayuda ndi Ahelene, amene anakhala ku Efeso; ndipo mantha anagwera onsewo, ndipo dzina la Yesu Iinakuzika.
18 Ndipo ambiri a iwo akukhulipirawo anadza, nabvomereza, nafotokoza macitidwe ao.
19 Ndipo ambiri a iwo akucita zamatsenga anasonkhanitsa mabuku ao, nawatentha pamaso pa onse; ndipo anawerenga mtengo wace, napeza ndalama zasiliva zikwi makumi asanu.
20 Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika.
21 Ndipo zitatha izi, Paulo anatsimikiza mu mzimu wace, atapita pa Makedoniya ndi Akaya, kunka ku Yerusalemu, kuti, Nditamuka komweko ndiyenera kuonanso ku Roma.