20 Koma Petro anati kwa iye, Ndalama yako itayike nawe, cifukwa unalingirira kulandira mphatso ya Mulungu ndi ndalama.
21 Ulibe gawo kapena colandira ndi mau awa; pakuti mtima wako suli wolunjika pamaso pa Mulungu.
22 Cifukwa: cace lapa coipa calm ici, pemphera Ambuye, kuti kapena akukhululukire iwe colingiriraca mtima wako.
23 Pakuti ndiona kuti wagwidwa ndi ndulu yowawa ndi nsinga ya cosalungama.
24 Ndipo Simoni anayankha nati, Mundipempherere ine kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.
25 Pamenepo iwo, atatha kucita umboni ndi kulankhula mau a Ambuye, anabwerakunkaku Yerusalemu, nalalikira Uthenga Wabwi no ku midzi yambirl ya Asamariya.
26 Koma mngelo wa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, nupite mbali ya kumwela, kutsata njira yotsika kucokera ku Yerusalemu kunka ku Gaza; ndiyo ya cipululu.