10 Ndipo Davide anafunsira kwa Mulungu, kun, Ndikwere kodi kuyambana ndi Afilisti? mudzawapereka m'dzanja langa kodi? Ndipo Yehova anati kwa iye, Kwera, pakuti ndidzawapereka m'dzanja lako.
11 Atafika tsono ku Baala Perazimu, Davide anawakantha komweko; nati Davide, Mulungu anapasula adani anga ndi dzanja langa, ngati pokhamulira madzi. Cifukwa cace analicha dzina la malowo Baala Perazimu.
12 Ndipo anasiyako milungu yao; nalamula Davide, ndipo anaitentha ndi moto.
13 Ndipo Afilisti anabwerezanso, nafalikira m'cigwamo.
14 Ndipo Davide anafunsiranso kwa Mulungu, nanena Mulungu naye, Usakwera kuwatsata, uwazungulire, nuwadzere pandunji pa mitengo ya mkandankhuku.
15 Ndipo kudzali, pakumva iwe kuwayula kunsonga kwa mitengo ya mkandankhuku, pamenepo uturukire kunkhondo; pakuti Mulungu waturukira pamaso pako kukantha gulu la Afilisti.
16 Nacita Davide monga Yehova adamuuza, nakantha gulu la Afilisti kuyambira ku Gibeoni kufikira ku Gezeri.