14 Pamenepo Yoabu ndi anthu anali naye anayandikira pamaso pa Aaramu kulimbana nao, ndipo anawathawa.
15 Ndipo pakuona ana a Amoni kuti adathawa Aaramu, iwo omwe anathawa pamaso pa Abisai mbale wace, nalowa m'mudzi. Pamenepo Yoabu anadza ku Yerusalemu.
16 Ndipo pakuona Aaramu kuti Israyeli anawakantha, anatumiza mithenga, naturuka nao Aaramu akukhala tsidya lija la mtsinjewo; ndi Sofaki kazembe wa khamu la Hadarezeri anawatsogolera.
17 Ndipo anamuuza Davide; namemeza iye Aisrayeli onse, naoloka Yordano, nawadzera, nanika nkhondo ayambane nao. Atandandalitsa nkhondo Davide kuyambana ndi Aaramu, anaponyana naye.
18 Ndipo Aaramu anathawa pamaso pa Israyeli; ndipo Davide anapha Aaramu apamagareta zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi anai; napha Sofaki kazembe wa khamulo.
19 Ndipo pakuona anyamata a Hadarezeri kuti Israyeli anawakantha, anapangana mtendere ndi Davide, namtumikira; ndi Aaramu anakana kuthandizanso ana a Amoni.