1 Ndipo Rehabiamu anamuka ku Sekemu; pakuti Aisrayeli onse adadza ku Sekemu kumlonga ufumu.
2 Ndipo kunali, atamva Yerobiamu mwana wa Nebati (popeza anali m'Aigupto kumene adathawira, kuthawa Solomo mfumu), Yerobiamu anabwera kucoka ku Aigupto.
3 Ndipo anatuma munthu kukamuitana, nadza Yerobiamu ndi Aisrayeli onse, nalankhula ndi Rehabiamu, ndi kuti,
4 Atate wanu analemeretsa goli lathu; inu tsono pepuzaniko nchito yolemetsa ya atate wanu, ndi goli lace lolemera anatisenzetsali, ndipo tidzakutumikirani.
5 Ndipo ananena nao, Mubwerenso atapita masiku atatu. Nacoka anthu.
6 Ndipo Rehabiamu mfumu anafunsana ndi akulu akulu, amene anaimirira pamaso pa Solomo atate wace akali ndi moyo, nati, Mundipangire bwanji, kuti ndiwabwezere mau anthu awa?
7 Ndipo ananena naye, kuti, Mukawacitira cokoma anthu awa, ndi kuwakonda, ndi kulankhula nao mau okoma, adzakhala anyamata anu kosatha.