18 Ndipo Yehosafati anawerama mutu wace, nkhope yace pansi; ndi Ayuda onse, ndi okhala m'Yerusalemu anagwa pansi pamaso pa Yehova, nalambira Yehova.
19 Ndipo Alevi, a ana a Akohati, ndi a ana a Kora, anauka kulemekeza Yehova Mulungu wa Israyeli ndi mau omveketsa.
20 Nalawira mamawa, naturuka kumka ku cipululu ca Tekoa; ndipo poturuka iwo, Yehosafati anakhala ciriri, nati, Mundimvere ine, Ayuda inu, ndi inu okhala m'Yerusalemu, Hmbikani mwa Yehova Mulungu wanu, ndipo mudzakhazikika; khulupirirani aneneri ace, ndipo mudzalemerera.
21 Ndipo atafunsana ndi anthu, anaika oyimbira Yehova, ndi kulemekeza ciyero cokometsetsa, pakuturuka iwo kutsogolera khamu la nkhondo, ndi kuti, Yamikani Yehova, pakuti cifundo cace cikhala cosatha.
22 Ndipo poyamba iwo kuyimba, ndi kulemekeza Yehova, anaika olalira alalire Aamoni, Amoabu, ndi a m'phiri la Seiri, akudzera Ayuda; ndipo anawakantha.
23 Pakuti ana a Amoni, ndi a Moabu, anaukira okhala m'phiri la Seiri, kuwapha ndi kuwaononga psiti; ndipo atatha okhala m'Seiri, anasandulikirana kuonongana.
24 Ndipo pofika Ayuda ku dindiro la kucipululu, anapenyera aunyinjiwo; taonani, mitembo iri ngundangunda, wosapulumuka ndi mmodzi yense.