26 Ndi tsiku lacinai anasonkhana m'cigwa ca Beraka; pakuti pamenepo analemekeza Yehova; cifukwa cace anacha dzina lace la malowo, Cigwa ca Beraka, mpaka lero lino.
27 Pamenepo anabwerera amuna onse a Yuda, ndi a ku Yerusalemu, nawatsogolera ndi Yehosafati, kubwerera kumka ku Yerusalemu ndi cimwemwe; pakuti Yehova anawakondweretsa pa adani ao.
28 Ndipo anafika ku Yerusalemu ndi zisakasa, ndi azeze, ndi malipenga, ku nyumba ya Yehova.
29 Ndipo kuopsa kwa Mulungu kunagwera maufumu onse a m'maiko, pamene anamva kuti Yehova adayambana ndi adani a Israyeli.
30 Nucita bata ufumu wa Yehosafati; pakuti Mulungu wace anampumulitsira pozungulirapo.
31 Momwemo Yehosafati anakhala mfumu ya Yuda; anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri; ndi dzina la mace ndiye Azuba mwana wa Sili.
32 Ndipo anayenda m'njira ya Asa atate wace osapambukamo, nacita zoongoka pamaso pa Yehova.