24 Pakuti khamu la nkhondo la Aaramu linadza la anthu owerengeka; ndipo Yehova anapereka khamu lalikuru m'dzanja lao; popeza adasiya Yehova Mulungu wa makolo ao. Motero anacitira Yoasi zomlanga.
25 Ndipo atamcokera (popeza anamsiya wodwala nthenda zazikuru), anyamata ace anamcitira ciwembu, cifukwa ca mwazi wa ana a Yehoyada wansembe, namupha pakama pace, namwalira iye; ndipo anamuika m'mudzi wa Davide, koma osamuika m'manda a mafumu.
26 Omcitira ciwembu ndi awa: Zabadi, mwana wa Simeati wamkazi M-amoni; ndi Yozabadi, mwana wa Simiriti wamkazi Mmoabu.
27 Za ana ace tsono, ndi katundu wamkuru anamsenza, ndi kumanganso kwa nyumba ya Mulungu, taonani, zilembedwa m'buku lomasulira la mafumu. Ndipo Amaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.