1 Ahazi anali wa zaka makumi awiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi; koma sanacita zoongoka pamaso pa Yehova ngati Davide kholo lace,
2 koma anayenda m'njira za mafumu a Israyeli, napangiranso Abaala mafano oyenga,
3 Nafukizanso yekha m'cigwa ca mwana wa Hinomu, napsereza ana ace m'moto, monga mwa zonyansa za amitundu, amene Yehova anawainga pamaso pa ana a Israyeli.
4 Naphera nsembe, nafukiza kumisanje, ndi kuzitunda, ndi patsinde pa mtengo uli wonse wogudira.