17 Anayamba tsono kuipatula tsiku loyamba la mwezi woyamba, nafikira ku likole la Yehova tsiku lacisanu ndi citatu la mwezi, naipatula nyumba ya Yehova m'masiku asanu ndi atatu; natsiriza tsiku lakhumi ndi cisanu ndi cimodzi.
18 Pamenepo analowa m'katimo kwa mfumu Hezekiya, nati, Tayeretsa nyumba yonse ya Yehova, ndi guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi gome la mkate woonekera, ndi zipangizo zace zonse.
19 Zipangizo zonse zomwe adazitaya mfumu Ahazi m'ufumu wace m'kulakwa kwace kuja, tazikonza, ndi kuzipatula; ndipo taonani, ziri ku guwa la nsembe la Yehova.
20 Pamenepo mfumu Hezekiya analawira mamawa, nasonkhanitsa akalonga a m'mudzi, nakwera kumka ku nyumba ya Yehova.
21 Ndipoanabweranazong'ombe zisanundi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri, ndi atonde asanu ndi awiri, zikhale nsembe yaucimo ya ufumu, ndi ya malo opatulika, ndi ya Yuda. Ndipo anawauza ansembe ana a Aroni azipereke pa guwa la nsembe la Yehova.
22 Momwemo anapha ng'ombezo, ndi ansembe analandira mwazi, nauwaza pa guwa la nsembe, napha nkhosa zamphongozo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe; anaphanso ana a nkhosawo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe.
23 Pamenepo anayandikiza nao atonde a nsembe yaucimo pamaso pa mfumu ndi msonkhano; ndipo iwo anawasanjika manja ao,