23 Ndipo oponya anayang'anitsa mibvi pa mfumu Yosiya, niti mfumu kwa anyamata ace, Ndicotseni ndalasidwa ndithu.
24 Pamenepo anyamata ace anamturutsa m'gareta, namuika m'gareta waciwiri anali naye, nabwerera naye ku Yerusalemu; nafa iye naikidwa m'manda a makolo ace. Ayuda onse ndi Yerusalemu nalira Yosiya.
25 Ndipo Yeremiya anamlembera Yosiya nyimbo yomlira; ndi oyimbira onse, amuna ndi akazi, amanena za Yosiya nyimbo za maliro zao mpaka lero lino; naziika zikhale lemba m'Israyeli; taonani, zilembedwa m'Nyimbo za Maliro.
26 Macitidwe ena tsono a Yosiya, ndi nchito zace zokoma, monga mulembedwa m'cilamulo ca Yehova,
27 ndi zocita iye, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zilembedwa m'buku la mafumu a Israyeli ndi Yuda.