6 Ndipo anasonkhana atumwi ndi akuru kuti anene za mlanduwo.
7 Ndipo pamene panali mafunsano ambiri, Petro anaimirira, nati kwa iwo, Abale, mudziwa kuti poyamba Mulungu anasankha mwa inu, kuti m'kamwa mwanga amitundu amve mau a Uthenga Wabwino, nakhulupire.
8 Ndipo Mulungu, amene adziwa mtima, anawacitira umboni; nawapatsa Mzimu Woyera, monga anatipatsa ife;
9 ndipo sanalekanitsa ife ndi iwo, nayeretsa mitima yao m'cikhulupiriro.
10 Nanga bwanji tsopano mulikumuyesa Mulungu, kuti muike pa khosi la akuphunzira gori, limene sanatha kunyamula kapena makolo athu kapena ife?
11 Koma tikhulupira tidzapulumuka mwa cisomo ca Ambuye Yesu Kristu, monga iwo omwe.
12 Ndipo khamu lonse linatonthola; ndipo anamvera Bamaba ndi Paulo alikubwerezanso zizindikiro ndi zozizwitsa zimene Mulungu anacita nao pa amitundu.